Nsewu wabwino ndi msanamira ya chitukuko-Jooma

Ngati njira imodzi yofuna kuchepetsa ngozi  mu nseu wa Mangochi-Monkey-bay, phungu wa dera la Monkey bay, a Ralph Jooma ayamba ntchito yokonza nseu-wu yomwe ndi ya ndalama zokwana pafupifupi 2 million kwacha.

Poyankhula ndi a Jooma, iwo ati kupatula kuchititsa ngozi, kuonongeka kwa nsewu wa Mangochi-Monkeybay kwakhala kukubweretsa mavuto osiyanasiyana  monga kukwera mtengo kwa maulendo a pa nseu,  kubwerela m’mbuyo kwa ntchito zokopa alendo, komanso kuonongeka kwa katundu monga nsomba zisanafike pa nsika kaamba kochedwa pa nseuwu.

Iwo anati akhala akupereka madando a vuto la kuonongeka kwa nseuwu ku  boma m’nyumba ya malamulo koma mpaka pano sanalandirebe yankho.

Nseuwu umalumikiza madera monga Mangochi boma, Golomoti komanso Monkey bay pa ntchito za malonda, zokopa alendo ndi zina .

Related posts

Andale Achimayi awapempha kuti alemekezeke Ovota

Elephant kills a Man in Kwilasya Village

Moyo ukulimba: Malipiro sakuoneka