Home Featured MANGOCHI SIKUCHITA BWINO PA NKHANI YOSAMBA M’MANJA

MANGOCHI SIKUCHITA BWINO PA NKHANI YOSAMBA M’MANJA

by Peter Dziyende
0 comments

Mkulu owona mapulani a za chitukuko ku Mangochi a Chris Nawata ati nkhani yosamba m’manja yatsamira pakusintha kaganizidwe ndipo khonsoloyi ikudalira adindo ngati mafumu, atsogoleri a mabungwe komanso zipembedzo kuti kusamba m’manja nthawi zonse kukhale chikhalidwe.

M’mawu awo a gulupu a Matuwi am’dera la Senior Chief Mponda atsindika pochenjeza anthu kuti ku nyanja sikubafa kosambira kapena kuchitira chimbudzi ndipo alimbikitsa onse kumanga zimbudzi m’makomo mwawo mvula isanayambe.

Poyikapo mulomo pa nkhaniyi, katswiri wa za ukhondo ndikusintha chikhalidwe ku bungwe la WaterAid a Maria Soko ati kusintha kaganizidwe sintchito ya tsiku limodzi ndipo mavuto a zachilengedwe ngati anamondwe komanso miliri yomwe boma la Mangochi lakumana nawo m’zaka ziwiri zapitazi ndiomwe akokera pansi ntchito zolimbitsa ukhondo.

Bungwe la WaterAid likugwira ntchito zake zolimbikitsa ukhondo osamba m’manja ku Nangalamu m’dera la mfumu yaikulu Bwananyambi komanso kwa Senior Chief Nankumba m’boma la Mangochi.

You may also like

Leave a Comment

Dzimwe Community Radio is nonprofit making institution currently located behind the Community Resource Centre Hall to the South East of Monkey Bay Airstrip. The radio was established in 1998 initially funded by UNITED NATION EDUCATION SCIENTIFIC AND CULTURE ORGANISATION (UNESCO) to act as a platform where people can discuss issues and find lasting solutions that concern them to achieve sustainable development.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00