Home Featured Zina ukaona: Kamba anga Mwala

Zina ukaona: Kamba anga Mwala

by Peter Dziyende
0 comments

Anthu ochuluka lero, 2 April 2025, mamawa anakhamukira ku msika wa Sumbi ku Monkey Bay m’boma la Mangochi komwe amakaona mnyamata wina wa zaka za pakati pa 20 ndi 30 yemwe ali mu ululu oopsa atachita za chisembwele ndi mkazi wa mwini ku Makanjira m’boma lomweli.

Mnyamatayu yemwe timutchule kuti John Chimtengo ,lomwe si dzina lake leni-leni anauza anthu omwe amuyang’anira kuti pa 28 March chaka chino anagona ndi mkazi yemwe mwamuna wake ali mdziko la South Africa.

John akuti izi zitachitika anabwelera kwa Sumbi ali bwinobwino koma patadutsa masiku ochepa ndipamene iye anayamba kuona zizindikiro zachilendo ku malo ake obisika ndipo pofika nthawi yomwe timafika pa msika wa Sumbi pomwe m’nyamatayu amapempha thandizo kuti abwelere ku mudzi kwawo,ndikuti atavulala kwambiri ku malo ake obisika.

Mnyamatayu anatinso akafuna kutaya madzi,akumatulutsa nsomba za mtundu wa usipa m’malo mwa mkozo.

Pakadalipano anthu akufuna kwabwino amuthandiza mnyamatayu ndipo wanyamuka ulendo opita kwawo ku Phalombe.

You may also like

Leave a Comment

Dzimwe Community Radio is nonprofit making institution currently located behind the Community Resource Centre Hall to the South East of Monkey Bay Airstrip. The radio was established in 1998 initially funded by UNITED NATION EDUCATION SCIENTIFIC AND CULTURE ORGANISATION (UNESCO) to act as a platform where people can discuss issues and find lasting solutions that concern them to achieve sustainable development.

Newsletter

Subscribe my Newsletter for new blog posts, tips & new photos. Let's stay updated!

@2025 – All Right Reserved. MACRA Community Radios

Are you sure want to unlock this post?
Unlock left : 0
Are you sure want to cancel subscription?
-
00:00
00:00
Update Required Flash plugin
-
00:00
00:00